24 Atsogoleri a Alevi anali Hasabiya, Serebiya ndi Yesuwa+ mwana wa Kadimiyeli.+ Ndipo abale awo ankaima moyangʼanizana nawo nʼkumatamanda ndi kuyamika Mulungu mogwirizana ndi malangizo a Davide,+ munthu wa Mulungu woona. Gulu lililonse la alonda linaima moyandikana ndi gulu lina la alonda.