31 Kenako ndinabwera ndi akalonga a Yuda pamwamba pa mpandawo. Ndinaikanso magulu akuluakulu awiri oimba nyimbo zoyamika Mulungu ndiponso magulu ena oti aziwatsatira pambuyo. Gulu lina la oimba linkayenda pampandawo mbali yakumanja kulowera ku Geti la Milu ya Phulusa.+