4 Tamverani! Mʼmapiri mukumveka phokoso la gulu la anthu.
Phokosolo likumveka ngati la anthu ambiri,
Tamverani! Kukumveka phokoso losonyeza kuti maufumu asokonezeka,
Phokoso la mitundu ya anthu imene yasonkhanitsidwa pamodzi.+
Yehova wa magulu ankhondo akumwamba akusonkhanitsira asilikali kunkhondo.+