17 Anthu 1,000 adzanjenjemera chifukwa choopsezedwa ndi munthu mmodzi.+
Mudzathawa chifukwa choopsezedwa ndi anthu 5
Moti ochepa amene adzatsale adzakhala ngati mtengo wautali wapangalawa wozikidwa pamwamba pa phiri,
Adzakhala ngati mtengo wachizindikiro wozikidwa paphiri lalingʼono.+