7 Yehova, Wowombola Isiraeli, Woyera wake,+ wauza amene amanyozedwa kwambiri,+ amene mtundu wa anthu umadana naye, mtumiki wa olamulira kuti:
“Mafumu adzaona nʼkuimirira,
Ndipo akalonga adzagwada pansi
Chifukwa cha Yehova yemwe ndi wokhulupirika,+
Woyera wa Isiraeli, amene wakusankha.”+