9 Chifukwa zilumba zidzayembekezera ine.+
Sitima zapamadzi za ku Tarisi zidzayembekezera ine ngati poyamba paja,
Kuti zikubweretsere ana ako aamuna kuchokera kutali,+
Atatenga siliva ndi golide wawo,
Kuti alemekeze dzina la Yehova Mulungu wako ndi Woyera wa Isiraeli,
Chifukwa iye adzakulemekeza.+