17 Iwo adzadya zokolola zanu ndi zakudya zanu.+
Adzadya ana anu aamuna ndi ana anu aakazi.
Adzadya nkhosa zanu ndi ngʼombe zanu.
Adzadya mitengo yanu ya mpesa ndi mitengo yanu ya mkuyu.
Iwo adzawononga ndi lupanga mizinda yanu imene mumaidalira, yokhala ndi mipanda yolimba kwambiri.”