23 Iwo adzagwira uta ndi nthungo.
Amenewa ndi anthu ankhanza ndipo sadzasonyeza chifundo.
Mawu awo adzamveka ngati mkokomo wa nyanja
Ndipo adzabwera pamahatchi.+
Iwo afola mwa dongosolo lomenyera nkhondo ngati mwamuna wankhondo kuti amenyane nawe, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni.”