9 Siliva amene anamusula kukhala mapalemapale amachokera ku Tarisi+ ndipo golide amachokera ku Ufazi.
Zonsezi zimakonzedwa mwaluso ndipo ndi ntchito ya manja a mmisiri wa zitsulo.
Amawaveka zovala zaulusi wabuluu ndi ubweya wa nkhosa wapepo.
Mafano onsewo amapangidwa ndi amisiri aluso.