5 Yehova wanena kuti,
‘Usalowe mʼnyumba imene olira maliro akuchitiramo phwando,
Ndipo usapite kukalira nawo maliro kapena kukapepesa.+
Chifukwa anthu awa ndawachotsera mtendere wanga,
Komanso chikondi changa chokhulupirika ndi chifundo changa,’ akutero Yehova.+