19 Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga komanso malo anga achitetezo,
Malo anga othawirako pa tsiku lamavuto,+
Mitundu ya anthu idzabwera kwa inu kuchokera kumalekezero a dziko lapansi,
Ndipo idzati: “Makolo athu analandira mafano monga cholowa chawo,
Analandira zinthu zachabechabe komanso zosapindulitsa.”+