11 Tsopano uza anthu a mu Yuda ndi anthu okhala mu Yerusalemu kuti, ‘Yehova wanena kuti: “Inetu ndikukukonzerani tsoka ndipo ndikuganizira njira yokulangirani. Chonde, bwererani nʼkusiya njira zanu zoipa. Sinthani zochita zanu ndi makhalidwe anu.”’”+