“Ndikusonkhanitsa anthu amʼmatenti a Yakobo amene anagwidwa nʼkutengedwa kupita kudziko lina,+
Ndipo ndidzamvera chisoni malo okhala a Yakobo.
Mzinda udzamangidwanso pamalo amene unali poyamba,+
Ndipo nsanja yokhala ndi mpanda wolimba idzakhala pamalo ake oyenerera.