-
Yeremiya 41:16Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
16 Ndiyeno Yohanani mwana wa Kareya ndi akuluakulu onse a asilikali amene anali naye anatenga anthu onse amene anatsala ku Mizipa. Anthu amenewa ndi amene anawapulumutsa mʼmanja mwa Isimaeli mwana wa Netaniya amene anawagwira atapha Gedaliya+ mwana wa Ahikamu. Anapulumutsa amuna, asilikali, akazi, ana ndi nduna zapanyumba ya mfumu ndipo anabwera nawo kuchokera ku Gibiyoni.
-