1 Yerusalemu amene anali ndi anthu ambiri tsopano watsala yekhayekha wopanda anthu.+
Amene anali ndi anthu ambiri poyerekeza ndi mitundu ina, wakhala ngati mkazi wamasiye.+
Amene anali wolemekezeka pakati pa zigawo zina wayamba kugwira ntchito yaukapolo.+