28 ngati utawaleza+ umene ukuoneka mumtambo pa tsiku la mvula. Umu ndi mmene kuwala kozungulira pamalopo kunkaonekera. Kunkaoneka ngati ulemerero wa Yehova.+ Nditaona zimenezo, ndinagwada nʼkuwerama mpaka nkhope yanga pansi. Kenako ndinayamba kumva mawu a winawake akulankhula.