14 Kenako ndinanena kuti: “Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, ndiloleni ndisachite zimenezo. Kuyambira ndili mwana mpaka pano sindinadzidetsepo podya nyama yopezeka itafa kapena nyama yochita kukhadzulidwa ndi chilombo,+ ndipo mʼkamwa mwanga simunalowepo nyama yodetsedwa.”+