8 Pamene amunawo ankapha anthu, ine ndekha ndi amene ndinatsala ndi moyo. Choncho ndinagwada nʼkuwerama mpaka nkhope yanga pansi ndipo ndinafuula kuti: “Mayo ine, Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa! Kodi muwononga anthu onse amene anatsala mu Isiraeli pamene mukukhuthulira ukali wanu pa Yerusalemu?”+