43 ‘Chifukwa sunakumbukire zimene ndinakuchitira uli wakhanda+ ndipo wandikwiyitsa pochita zinthu zonsezi, tsopano ndikubwezera mogwirizana ndi zochita zako. Ndipo sudzapitirizanso kuchita khalidwe lako lonyansa komanso zinthu zonse zonyansa zimene ukuchita,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.