5 Iwe pamodzi ndi nsomba zonse zamumtsinje wa Nailo ndidzakutayani mʼchipululu.
Mudzagwera panthaka yopanda chilichonse ndipo palibe amene adzakutengeni nʼkukakuikani mʼmanda.+
Ndidzakuperekani kwa zilombo zakutchire ndi mbalame zouluka mumlengalenga kuti mukhale chakudya chawo.+