12 Ndidzachititsa kuti gulu la anthu amene amakutsatira aphedwe ndi malupanga a asilikali amphamvu.
Onsewo ndi anthu a mitundu ina omwe ndi ankhanza kwambiri.+
Iwo adzawononga zinthu zimene Iguputo amazinyadira ndipo anthu ambiri amene amamutsatira adzaphedwa.+