2 Kenako Yehova anandiuza kuti: “Geti ili lipitiriza kukhala lotseka. Silikuyenera kutsegulidwa ndipo munthu aliyense sakuyenera kudzera pageti limeneli chifukwa chakuti Yehova, Mulungu wa Isiraeli, walowa kudzera pageti limeneli.+ Choncho likuyenera kukhala lotseka.