11 Kenako Aleviwo adzakhala atumiki mʼmalo anga opatulika kuti azidzayangʼanira mageti a kachisi+ komanso kutumikira pakachisi. Iwo azidzapha nyama za nsembe zopsereza zathunthu ndi nsembe zina za anthu ndipo adzaimirira pamaso pa anthuwo nʼkumawatumikira.