25 Mʼmwezi wa 7, kuyambira pa tsiku la 15 la mweziwo, kwa masiku 7 pa nthawi ya chikondwerero,+ mtsogoleri azipereka kwa wansembe zinthu zofanana ndi zimenezi. Azipereka zinthu zimenezi kuti zikhale nsembe yamachimo, nsembe zopsereza zathunthu, nsembe yambewu ndiponso mafuta.’”