18 Amenewa ndi maloto amene ine Mfumu Nebukadinezara ndinalota. Tsopano iwe Belitesazara umasulire malotowa, chifukwa amuna ena onse anzeru a mu ufumu wanga alephera kundiuza kumasulira kwake.+ Koma iwe ungathe kuwamasulira chifukwa mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe.’