24 Kenako mfumu inalamula kuti abweretse amuna amene ananenera Danieli zoipa aja. Atawabweretsa, anawaponya mʼdzenje la mikango pamodzi ndi ana awo komanso akazi awo. Iwo asanafike nʼkomwe pansi pa dzenjelo, mikango inawakhadzulakhadzula nʼkuphwanya mafupa awo onse.+