11 Yehova wanena kuti,
‘Chifukwa Edomu wandigalukira mobwerezabwereza,+ sindidzamusinthira chigamulo changa.
Chifukwa anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga,+
Komanso anakana kusonyeza chifundo.
Anapitiriza kuwakhadzulakhadzula,
Ndipo anapitirizabe kuwakwiyira kwambiri.+