20 Anthu amene anatengedwa pamalo okwera omenyerapo nkhondowa nʼkupita nawo kudziko lina,+
Amene ndi Aisiraeli, adzatenga dziko la Akanani mpaka kukafika ku Zarefati.+
Anthu amene anatengedwa kuchokera ku Yerusalemu, amene anali ku Sefaradi, adzatenga mizinda ya Negebu.+