23 “Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena kuti, ‘Pa tsiku limenelo ndidzakutenga iwe Zerubabele+ mwana wa Salatiyeli,+ mtumiki wanga,’ watero Yehova. ‘Ndipo ndidzachititsa kuti ukhale ngati mphete yodindira chifukwa iwe ndi amene ndakusankha,’ watero Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.”