5 Inu mudzathawira kuchigwa chimene chidzakhale pakati pa mapiri anga, chifukwa chigwacho chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa ngati mmene munathawira chivomerezi chimene chinachitika mʼmasiku a Uziya, mfumu ya Yuda.+ Ndipo Yehova Mulungu wanga adzabwera limodzi ndi oyera onse.+