10 “Ndipo ndani wa inu amene angatseke zitseko za kachisi popanda malipiro?+ Mukayatsa moto paguwa langa lansembe, mumafuna kulandira malipiro.+ Ine sindikukondwera nanu, ndipo nsembe zimene mukundipatsa ngati mphatso sizikundisangalatsa,”+ watero Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.