20 Iye anawayankha kuti: “Chifukwa cha kuchepa kwa chikhulupiriro chanu. Ndithu ndikukuuzani, ngati mutakhala ndi chikhulupiriro chofanana ndi kanjere ka mpiru kuchepa kwake, mudzatha kuuza phiri ili kuti, ‘Choka pano upite apo,’ ndipo lidzachokadi. Palibe chimene chidzakhale chosatheka kwa inu.”+