8 Choncho ngati dzanja lako kapena phazi lako limakupunthwitsa, ulidule nʼkulitaya kutali.+ Ndi bwino kuti ukapeze moyo ulibe chiwalo chimodzi kapena uli wolumala kusiyana nʼkuti uponyedwe mʼmoto wosatha uli ndi manja onse awiri kapena mapazi onse awiri.+