12 Kenako anayamba kulankhula nawo pogwiritsa ntchito mafanizo kuti: “Munthu wina analima munda wa mpesa+ nʼkumanga mpanda kuzungulira mundawo. Komanso anakumba dzenje loponderamo mphesa nʼkumanga nsanja.+ Atatero anausiya mʼmanja mwa alimi nʼkupita kudziko lina.+