42 Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumapereka chakhumi cha timbewu ta minti ndi ta luwe komanso cha mbewu zakudimba zamtundu uliwonse.+ Koma mumanyalanyaza chilungamo ndi chikondi cha Mulungu! Unali udindo wanu kuchita zinthu zimenezi, koma simumayenera kunyalanyaza zinthu zinazo.+