17 (Zimenezi nʼzogwirizana ndi zimene Malemba amanena kuti: “Ndakusankha kuti ukhale bambo wa mitundu yambiri.”)+ Izi zinali choncho pamaso pa Mulungu amene Abulahamu ankamukhulupirira, yemwenso amaukitsa akufa ndipo amanena za zinthu zimene palibe ngati kuti zilipo.