12 Mulungu anauza aneneriwo kuti sankadzitumikira okha, koma ankatumikira inuyo. Tsopano zinthu zimenezi zaululidwa ndi anthu omwe akulengeza uthenga wabwino kwa inu mothandizidwa ndi mzimu woyera wochokera kumwamba.+ Angelo amafunitsitsa atamvetsa zinthu zimenezi.