15 Ndiyeno Mose anapha+ ng’ombeyo, ndipo anatenga magazi+ ake ndi kuwapaka ndi chala chake panyanga zonse za guwa lansembe, n’kuyeretsa guwalo ku uchimo. Koma magazi otsalawo anawathira pansi pa guwa lansembe kuti alipatule, kuphimba machimo+ paguwalo.