21 Anatenganso matumbo ndi ziboda n’kuzitsuka ndi madzi. Ndiyeno Mose anatentha nkhosa yonseyo paguwa lansembe.+ Inali nsembe yopsereza yafungo lokhazika mtima pansi.+ Komanso, inali nsembe yotentha ndi moto yoperekedwa kwa Yehova, monga mmene Yehova analamulira Mose.