38 Amene anali kumanga msasa wawo kum’mawa kwa chihema chopatulika, kumbali yotulukira dzuwa, anali Mose ndi Aroni, ndiponso ana a Aroni. Ntchito yawo inali kutumikira m’malo opatulika,+ kutumikira ana a Isiraeli. Aliyense amene si Mlevi akayandikira malowo, anayenera kuphedwa.+