8 Mwana wa nkhosa wamphongo winayo muzim’pereka nsembe madzulo kuli kachisisira. Muzim’pereka limodzi ndi nsembe yambewu ndiponso yachakumwa, mofanana ndi nsembe ya m’mawa ija. Izikhala nsembe yotentha ndi moto yafungo lokhazika mtima pansi kwa Yehova.+