8 Pa tsikuli muzipereka nsembe yopsereza yafungo lokhazika mtima pansi kwa Yehova. Nsembeyo izikhala ya ng’ombe yaing’ono yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, ndi ana a nkhosa 7 amphongo, ndipo mwana wa nkhosa aliyense azikhala wachaka chimodzi.+ Muzionetsetsa kuti nyamazo n’zopanda chilema.+