12 Malo anga okhala ali ngati hema wa abusa. Mitengo yake yazulidwa ndipo hemayo wachotsedwapo.+
Ndakulunga moyo wanga ngati munthu wowomba nsalu.
Winawake wandidula+ ngati mmene amadulira nsalu kuchowombera nsalu akamaliza kuiwomba.
Kuyambira m’mawa mpaka usiku mumandipereka ku zowawa.+