12 Choncho ine ndidzakonzeratu zoti anthu inu mudzaphedwe ndi lupanga.+ Nonsenu mudzawerama kuti akupheni,+ popeza ndinakuitanani+ koma simunayankhe. Ndinalankhula koma simunamvere.+ Munapitiriza kuchita zinthu zoipa pamaso panga+ ndipo munasankha zinthu zimene sindisangalala nazo.”+