Mawu Akumapeto
^ [1] (ndime 3) Abale ndi alongo athu ena amalephera kusonkhana nthawi zonse chifukwa cha mavuto monga matenda aakulu. Abale ndi alongowa ayenera kudziwa kuti Yehova amamvetsa mavuto awo ndipo amayamikira zimene amayesetsa kuchita pomulambira. Akulu angapeze njira yothandizira abalewa. Mwachitsanzo, angawathandize kuti azimvetsera misonkhano pa foni kapena kuwajambulira kuti amvetsere ali kunyumba.