Mawu a M'munsi
a Ichi chimagwira ntchito m’maiko kumene kupita kocheza kumawonedwa kukhala kachitidwe koyenera kaamba ka Akristu. Nthawi zambiri mwamuna amayambirira, ngakhale kuti palibe chifukwa cha Malemba choletsa mkazi wachichepere kulongosola kudzimva kwake m’njira yodekha ngati mnyamata awoneka wa manyazi ndi wozengeleza.—Yerekezani ndi Nyimbo ya Solomo 8:6.