Mawu a M'munsi
b Nzowona kuti Chilamulo cha Mose chinalengeza mkazi wosamba kukhala “wodetsedwa.” (Levitiko 15:19-33) Koma chimenechi chinali kokha m’lingaliro lamwambo. Mwachiwonekere, malamuloŵa anatumikira kuphunzitsa ulemu wa kupatulika kwa mwazi. (Levitiko 17:10-12) Panthaŵi imodzimodziyo, malamulowo anatumikira kukumbutsa mtundu Wachiyuda kuti mtundu wa anthu ngobadwira mu uchimo ndipo umafunikira mombolo.