Mawu a M'munsi
b Mogwirizana ndi ripoti la tchalitchi lolembedwa ndi Canon Arboleya mu 1933, munthu wogwira ntchito analingalira tchalitchi kukhala chipangizo cha olemera ndi gulu la okhupuka chimene chinkamudyera masuku pamutu. Arboleya analongosola kuti: “Khamu linathaŵa Tchalitchi chifukwa chakuti linachikhulupirira kukhala mdani wawo wamkulu.”