Mawu a M'munsi
c Kwenikweni ansembe ena Achikatolika anamenya nkhondoyo m’magulu ankhondo a Franco. Wansembe wa ku Zafra, Extremadura, anali wotchuka kwambiri kaamba ka nkhalwe yake. Kumbali ina, ansembe oŵerengeka anatsutsa molimba mtima kuphedwa kwa onyumwiridwa kukhala omvera chisoni boma—ndipo chifupifupi munthu mmodzi anaphedwa kaamba ka chifukwa chimenechi. Kadinala Vidal y Barraquer, amene anayesa kusunga uchete mkati mwa nkhondo yonseyo, anakakamizika ndi boma la Franco kukhala m’dziko lachilendo kufikira imfa yake mu 1943.