Mawu a M'munsi
a Kuvomereza zolakwa kwina kunapangidwa pamsonkhano wa onse aŵiri ansembe ndi abishopu mu 1971. Ngakhale kuti mawuwo sanachirikizidwe ndi chiŵerengero chokulira chofunikira cha aŵiri mwa atatu, oposa theka anasaina mawu akuti: “Modzichepetsa tikuvomereza ndi kupempha chikhululukiro kuti sitinadziŵe mmene, ndi pamene tikadakhala ‘atumiki owona oyanjanitsa,’ pakati pa anthu akwathu okanthidwa ndi nkhondo ya kuphana kwa pachibale.”